12 “‘Pa tsiku la 15 la mwezi wa 7,+ muzichita msonkhano wopatulika.+ Musamagwire ntchito yolemetsa yamtundu uliwonse.+ Muzichita chikondwerero kwa Yehova masiku 7.+
18 Ndiyeno tsiku ndi tsiku, kuchokera tsiku loyamba mpaka tsiku lomaliza, anali kuwerenga mokweza buku la chilamulo cha Mulungu woona.+ Iwo anachita chikondwererocho masiku 7, ndipo pa tsiku la 8 anachita msonkhano wapadera malinga ndi lamulo.+