11 Pakuti m’masiku 6 Yehova anapanga kumwamba, dziko lapansi, nyanja, ndi zonse zili mmenemo,+ ndipo anayamba kupuma pa tsiku la 7.+ N’chifukwa chake Yehova anadalitsa tsiku la sabata ndi kulipanga kukhala lopatulika.+
13 “Koma iwe uuze ana a Isiraeli kuti, ‘Muonetsetse kuti muzisunga masiku anga a sabata,+ pakuti ndi chizindikiro pakati pa ine ndi inu m’mibadwo yanu yonse, kuti mudziwe kuti ine Yehova ndakusankhani kukhala opatulika.+