12 Ndipo muzisangalala pamaso pa Yehova Mulungu wanu,+ inuyo ndi ana anu aamuna, ana anu aakazi, akapolo anu aamuna, akapolo anu aakazi ndi Mlevi wokhala mumzinda wanu, chifukwa iye alibe gawo kapena cholowa monga inu.+
14 Fuko la Alevi lokha ndi limene sanalipatse cholowa cha malo.+ Cholowa chawo ndicho nsembe zotentha ndi moto+ zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wa Isiraeli, monga mmene anawalonjezera.+