20 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Aroni, kuti: “Iwe udzakhala wopanda cholowa m’dziko mwawo, ndipo sudzapatsidwa gawo lililonse pakati pawo.+ Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa ana a Isiraeli.+
12 Ndipo muzisangalala pamaso pa Yehova Mulungu wanu,+ inuyo ndi ana anu aamuna, ana anu aakazi, akapolo anu aamuna, akapolo anu aakazi ndi Mlevi wokhala mumzinda wanu, chifukwa iye alibe gawo kapena cholowa monga inu.+