10Ndiyeno Nadabu ndi Abihu,+ ana a Aroni, aliyense anatenga chofukizira,+ n’kuikamo moto ndi zofukiza+ pamwamba pake. Pamenepo anayamba kupereka zofukiza pamoto wosaloledwa+ ndi Yehova, umene iye sanawalamule.
38 zofukizira za amuna amene anafa+ chifukwa cha kuchimwa. Azisule kuti zikhale timalata topyapyala n’kukutira nato guwa lansembe,+ popeza anafika nazo pamaso pa Yehova, ndipo zakhala zopatulika. Timalatato tikhale chikumbutso kwa ana a Isiraeli.’”+