16 pamenepo ine ndidzakuchitani zotsatirazi: pokulangani ndidzakugwetserani zoopsa za chifuwa chachikulu+ ndi kuphwanya kwa thupi koopsa, kumene kudzachititsa maso anu khungu+ ndi kukufooketsani.+ Simudzapindula ndi mbewu zimene mwafesa, chifukwa adani anu adzadya zokolola zanuzo.+
17 Iwo adzadya zokolola zanu ndi mkate wanu.+ Amuna amenewo adzadya ana anu aamuna ndi ana anu aakazi. Adzadya nkhosa zanu ndi ng’ombe zanu. Adzadya mtengo wanu wa mpesa ndi mtengo wanu wa mkuyu.+ Iwo adzagwetsa ndi lupanga mizinda yanu imene mumaidalira, yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri.”