Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 26:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 pamenepo ine ndidzakuchitani zotsatirazi: pokulangani ndidzakugwetserani zoopsa za chifuwa chachikulu+ ndi kuphwanya kwa thupi koopsa, kumene kudzachititsa maso anu khungu+ ndi kukufooketsani.+ Simudzapindula ndi mbewu zimene mwafesa, chifukwa adani anu adzadya zokolola zanuzo.+

  • Deuteronomo 28:51
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 51 Iwo adzadya chipatso cha ziweto zako ndi zipatso za nthaka yako kufikira utafafanizidwa,+ ndipo sadzakusiyirako mbewu, vinyo watsopano kapena mafuta, mwana wa ng’ombe yako kapena mwana wa nkhosa yako kufikira atakuwonongeratu.+

  • Nehemiya 9:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Zokolola za m’dzikoli zachulukira+ mafumu+ amene mwatiikira chifukwa cha machimo athu.+ Iwo akulamulira matupi athu komanso ziweto zathu mmene akufunira, ndipo tili pamavuto aakulu.+

  • Yesaya 1:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Dziko lanu lawonongedwa.+ Mizinda yanu yatenthedwa ndi moto,+ ndipo alendo akudya zokolola zochokera munthaka yanu, inu mukuona.+ Chilichonse chawonongeka ngati mmene zimakhalira adani akalanda dziko.+

  • Yeremiya 5:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Iwo adzadya zokolola zanu ndi mkate wanu.+ Amuna amenewo adzadya ana anu aamuna ndi ana anu aakazi. Adzadya nkhosa zanu ndi ng’ombe zanu. Adzadya mtengo wanu wa mpesa ndi mtengo wanu wa mkuyu.+ Iwo adzagwetsa ndi lupanga mizinda yanu imene mumaidalira, yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena