8 Chotero ana a Isiraeliwo anachita monga mmene Yoswa anawalamulira. Anapita pakati pa mtsinje wa Yorodano, ndipo anakanyamula miyala 12 mogwirizana ndi chiwerengero cha mafuko a ana a Isiraeli,+ monga mmene Yehova analamulira Yoswa. Ananyamula miyalayo ndi kukaiika kumalo awo ogona.+