5 Ndiyeno iye anapempha amuna a ku Sukoti+ kuti: “Chonde, patsaniko anthu amene akunditsatirawa+ mitanda yobulungira ya mkate chifukwa ndi otopa, pakuti ndikuthamangitsa Zeba+ ndi Zalimuna,+ mafumu a Midiyani.”
12 Munthu wogoba zitsulo ndi chogobera watentha chitsulocho ndi makala amoto. Wachiwongola ndi nyundo, ndipo wakhala ali jijirijijiri kuchiumba ndi dzanja lake lamphamvu.+ Wamva njala ndipo alibe mphamvu. Sanamwe madzi, chotero watopa.