15 Ineyo ndinatamanda kusangalala,+ chifukwa palibe chabwino chimene anthu angachite padziko lapansi pano kuposa kudya, kumwa ndi kusangalala, pamene akugwira ntchito mwakhama masiku onse a moyo wawo,+ amene Mulungu woona wawapatsa padziko lapansi pano.+