Oweruza 9:54 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 54 Msangamsanga Abimeleki anaitana mtumiki wake womunyamulira zida ndi kumuuza kuti: “Tenga lupanga lako undiphe,+ kuopera kuti anthu anganene za ine kuti, ‘Anaphedwa ndi mkazi.’” Nthawi yomweyo, mtumiki wakeyo anamubaya* ndi lupanga, ndipo anafa.+ 1 Samueli 31:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+ 2 Samueli 17:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 Koma Ahitofeli ataona kuti malangizo ake sanawagwiritse ntchito,+ anakwera bulu wake ndi kunyamuka kupita kunyumba yake kumzinda wakwawo.+ Kenako anakonzekeretsa banja lake+ ndipo anadzimangirira+ moti anafa.+ Chotero anaikidwa m’manda+ a makolo ake. Mateyu 27:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Choncho iye anaponya ndalama zasiliva zija m’kachisi n’kuchoka, ndipo anakadzimangirira.+
54 Msangamsanga Abimeleki anaitana mtumiki wake womunyamulira zida ndi kumuuza kuti: “Tenga lupanga lako undiphe,+ kuopera kuti anthu anganene za ine kuti, ‘Anaphedwa ndi mkazi.’” Nthawi yomweyo, mtumiki wakeyo anamubaya* ndi lupanga, ndipo anafa.+
4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+
23 Koma Ahitofeli ataona kuti malangizo ake sanawagwiritse ntchito,+ anakwera bulu wake ndi kunyamuka kupita kunyumba yake kumzinda wakwawo.+ Kenako anakonzekeretsa banja lake+ ndipo anadzimangirira+ moti anafa.+ Chotero anaikidwa m’manda+ a makolo ake.