7 “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndidzatumiza Nebukadirezara mfumu ya Babulo, mfumu ya mafumu,+ kuchokera kumpoto+ kuti akaukire Turo. Iye adzapita ndi mahatchi,+ magaleta ankhondo,+ asilikali a pamahatchi, khamu la anthu+ kapena kuti gulu lalikulu la anthu.