-
1 Samueli 7:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Zitatero, Samueli anauza nyumba yonse ya Isiraeli kuti: “Ngati mukubwereradi kwa Yehova+ ndi mtima wanu wonse, chotsani milungu yachilendo pakati panu.+ Muchotsenso zifaniziro za Asitoreti,+ ndi kulunjikitsa mitima yanu kwa Yehova mosayang’ananso kwina,+ ndi kutumikira iye yekha. Mukatero, adzakupulumutsani m’manja mwa Afilisiti.”+
-
-
2 Mbiri 15:8Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Asa atangomva mawu amenewa ndi ulosi wa mneneri Odedi,+ analimba mtima n’kuyamba kuchotsa zinthu zonyansa+ m’dziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi m’mizinda imene analanda m’dera lamapiri la Efuraimu.+ Anayambanso kukonza guwa lansembe la Yehova limene linali patsogolo pa khonde la nyumba ya Yehova.+
-