5 Davide pamodzi ndi nyumba yonse ya Isiraeli anali kusangalala pamaso pa Yehova, akuimba mitundu yonse ya zoimbira za mtengo wofanana ndi mtengo wa mkungudza. Anali kuimbanso zeze,+ zoimbira za zingwe,+ zinganga+ ndi maseche+ osiyanasiyana.
12 Mfumuyo inapanga zochirikizira nyumba ya Yehova+ ndi nyumba ya mfumu, pogwiritsira ntchito matabwa a m’bawawo. Inapanganso azeze+ ndi zoimbira za zingwe+ n’kupatsa oimba. Matabwa a m’bawa ochuluka chonchi sanayambe abwerapo kapena kuonedwapo mpaka lero.