25 Asilikaliwo atachoka (popeza anamusiya akuvutika kwambiri),+ atumiki ake anam’konzera chiwembu+ chifukwa cha magazi+ a ana a wansembe Yehoyada+ ndipo anamuphera pabedi+ lake. Kenako anamuika m’manda mu Mzinda wa Davide+ koma sanamuike m’manda a mafumu.+
29 “Amuna inu, abale anga, ndilankhula ndithu mwaufulu za kholo lathu Davide. Iye anamwalira+ ndi kuikidwa m’manda, ndipo manda ake tili nawo mpaka lero.