10 Iyeyo ndi amene adzamanga nyumba ya dzina langa.+ Adzakhala mwana+ wanga, ndipo ine ndidzakhala atate wake.+ Ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu+ pa Isiraeli ndipo sudzagwedezeka mpaka kalekale.’
39 Choncho atapita patsogolo pang’ono, anagwada mpaka nkhope yake pansi, ndipo anapemphera+ kuti: “Atate wanga, ngati n’kotheka, kapu+ iyi indipitirire. Koma osati mwa kufuna kwanga,+ koma mwa kufuna kwanu.”+