20 Azichita zimenezi kuti mtima wake usadzikweze pamaso pa abale ake,+ komanso kuti asachoke pachilamulo mwa kupatukira kudzanja lamanja kapena lamanzere.+ Azichita zimenezi kuti iyeyo ndi ana ake atalikitse masiku a ufumu wawo+ mu Isiraeli.
9 Mawu onsewa anthu adzawadziwa.+ Efuraimu ndi anthu okhala ku Samariya,+ adzawadziwa mawuwo chifukwa cha kudzikweza kwawo ndiponso chifukwa cha mwano wa mumtima mwawo. Pakuti iwo anena kuti:+
20 Koma pamene mtima wake unayamba kudzitukumula ndiponso pamene anaumitsa mtima wake ndi kuchita zinthu modzikweza,+ anatsitsidwa pampando wake wachifumu ndipo ulemerero wake unachotsedwa.+