Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 4:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Pachifukwa chimenechi valani ziguduli,* anthu inu.+ Dzigugudeni pachifuwa ndi kulira mofuula,+ chifukwa mkwiyo woyaka moto wa Yehova sunatichokere.+

  • Maliro 2:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala pansi ndipo akhala chete.+

      Iwo athira fumbi pamitu+ yawo ndipo avala ziguduli.*+

      Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo mpaka padothi.+

  • Yoweli 1:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Lirani momvetsa chisoni ngati mmene amalirira namwali amene wavala chiguduli*+ polirira mwamuna amene anali kufuna kumukwatira.

  • Amosi 8:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndidzasandutsa zikondwerero zanu kukhala maliro+ ndipo nyimbo zanu zonse zidzakhala nyimbo zoimba polira. Ndidzachititsa kuti anthu onse avale ziguduli* ndipo mitu yonse idzametedwa mpala.+ Ndidzachititsa kuti zochitika pa tsikulo zikhale ngati maliro a mwana wamwamuna mmodzi yekhayo amene wamwalira,+ moti tsiku la mapeto a zinthu zonsezi lidzakhala lowawa.’

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena