17 “Anthu inu mwatopetsa Yehova ndi mawu anu,+ ndipo mwanena kuti, ‘Tamutopetsa motani?’ Mwa kunena kuti, ‘Aliyense wochita zoipa ndi wabwino kwa Yehova, ndipo iye amakondwera ndi anthu otero.’+ Kapena mwa kunena kuti, ‘Kodi Mulungu wachilungamo ali kuti?’”+