7 Ndidzawapatsa mtima wodziwa kuti ine ndine Yehova.+ Iwo adzakhala anthu anga+ ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo pakuti adzabwerera kwa ine ndi mtima wawo wonse.+
33 “Pangano+ limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili:+ Ndidzaika chilamulo changa mwa iwo+ ndipo ndidzachilemba mumtima mwawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,”+ watero Yehova.
5 Mtundu uliwonse wa anthu udzayenda m’dzina la mulungu wake.+ Koma ife tidzayenda m’dzina la Yehova Mulungu wathu+ mpaka kalekale, inde mpaka muyaya.+