5 Aneneriwo anali kukuuzani kuti, ‘Chonde, aliyense wa inu atembenuke ndi kusiya njira yake yoipa ndi zochita zake zoipa+ kuti mupitirize kukhala m’dziko limene Yehova anakupatsani, inuyo ndi makolo anu. Anakupatsani dzikoli kuti chikhale cholowa chanu kwa nthawi yaitali.+