9 “Ngakhale Manda+ amene ali pansi agwedezeka kuti akumane nawe ukamabwera. Chifukwa cha iwe, mandawo adzutsa akufa,+ adzutsa olamulira onse a padziko lapansi okhala ngati mbuzi.+ Achititsa mafumu onse a mitundu ya anthu kunyamuka pamipando yawo yachifumu.+