8 Pamene amunawo anali kupha anthu, ine ndinatsala ndekha wamoyo, ndipo ndinagwada n’kuwerama mpaka nkhope yanga pansi.+ Kenako ndinafuula kuti: “Kalanga ine,+ Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa! Kodi muwononga otsala onse a Isiraeli pamene mukukhuthulira ukali wanu pa Yerusalemu?”+