3 “‘Fuula+ iwe Hesiboni+ pakuti mzinda wa Ai wafunkhidwa zinthu zake! Lirani inu midzi yozungulira Raba. Valani ziguduli.+ Lirani mokuwa ndi kuyendayenda m’makola amiyala chifukwa Malikamu adzatengedwa kupita ku ukapolo+ pamodzi ndi ansembe ndi akalonga ake onse.+