4 “M’masiku amenewo ndiponso pa nthawi imeneyo+ ana a Isiraeli pamodzi ndi ana a Yuda adzabwera,”+ watero Yehova. “Iwo adzayenda akulira+ ndipo adzafunafuna Yehova Mulungu wawo.+
6 Ndidzachititsa nyumba ya Yuda kukhala yapamwamba ndipo nyumba ya Yosefe ndidzaipulumutsa.+ Ndidzawachitira chifundo ndipo ndidzawapatsa malo okhala.+ Iwo adzakhala ngati sanakanidwepo chiyambire.+ Pakuti ine ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.+