18 “M’masiku amenewo nyumba ya Yuda idzayenda pamodzi ndi nyumba ya Isiraeli,+ ndipo onse+ adzatuluka m’dziko la kumpoto ndi kulowa m’dziko limene ndinapereka kwa makolo anu monga cholowa chawo.+
16 “Koma iwe mwana wa munthu, tenga ndodo+ ndi kulembapo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi anzake, ana a Isiraeli.’+ Utengenso ndodo ina ndi kulembapo kuti, ‘Ndodo ya Yosefe yoimira Efuraimu+ komanso anzawo onse a nyumba ya Isiraeli.’+