-
2 Mbiri 36:23Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
23 “Koresi mfumu ya Perisiya+ wanena kuti, ‘Yehova Mulungu wakumwamba wandipatsa+ maufumu onse a padziko lapansi. Iye wandituma kuti ndim’mangire nyumba ku Yerusalemu m’dziko la Yuda.+ Aliyense amene ali pakati panu mwa anthu onse amene amamutumikira,+ Yehova Mulungu wake akhale naye.+ Choncho apite.’”+
-
-
Ezekieli 37:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Uwauze kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine nditenga ndodo ya Yosefe imene ili m’dzanja la Efuraimu. Ndodo imeneyi ikuimiranso mafuko a Isiraeli omwe ndi anzake a Efuraimu. Ndidzaika mafukowo pandodo ya Yuda ndipo ndodo ziwirizo zidzakhala ndodo imodzi.+ Ndodozo zidzakhala ndodo imodzi m’dzanja langa.”’
-