-
Danieli 4:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 “Pa nthawi imeneyo Danieli, wotchedwa Belitesazara,+ anada nkhawa kwa kanthawi ndipo anachita mantha.+
“Chotero mfumuyo inamuuza kuti, ‘Iwe Belitesazara, malotowa ndi kumasulira kwake zisakuchititse mantha.’+
“Belitesazara anayankha kuti, ‘Inu mbuyanga, zikanakhala bwino malotowa akanakhala okhudza anthu amene amadana nanu. Zikanakhalanso bwino kumasulira kwake kukanakhala kokhudza adani anu.+
-
-
Danieli 4:33Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
33 Nthawi yomweyo+ mawuwa anakwaniritsidwa pa Nebukadinezara ndipo anathamangitsidwa pakati pa anthu. Iye anayamba kudya udzu ngati ng’ombe ndipo thupi lake linkanyowa ndi mame akumwamba. Tsitsi lake linatalika kwambiri ngati nthenga za chiwombankhanga ndipo zikhadabo zake zinatalika ngati za mbalame.+
-