16 Pa nthawi imeneyo anthu oopa Yehova+ analankhulana, aliyense ndi mnzake, ndipo Yehova anatchera khutu ndi kumvetsera.+ Buku la chikumbutso linayamba kulembedwa pamaso pake.+ Buku limeneli linali lonena za anthu oopa Yehova ndi anthu amene anali kuganizira za dzina lake.+
5 Choncho amene wapambana pa nkhondo+ adzavekedwa malaya akunja oyera.+ Ndipo sindidzafafaniza dzina lake m’buku la moyo,+ koma ndidzavomereza dzina lake pamaso pa Atate wanga,+ ndi pamaso pa angelo ake.+