36 Kwa masiku 7 muzipereka nsembe yotentha ndi moto kwa Yehova. Pa tsiku la 8 muzichita msonkhano wopatulika,+ ndipo muzipereka nsembe yotentha ndi moto kwa Yehova. Umenewu ndi msonkhano wapadera. Musagwire ntchito iliyonse yolemetsa.
18 Ndiyeno tsiku ndi tsiku, kuchokera tsiku loyamba mpaka tsiku lomaliza, anali kuwerenga mokweza buku la chilamulo cha Mulungu woona.+ Iwo anachita chikondwererocho masiku 7, ndipo pa tsiku la 8 anachita msonkhano wapadera malinga ndi lamulo.+