4 “Inu anthu anga, tandimverani. Iwe mtundu wanga,+ tatchera khutu kwa ine. Pakuti kwa ine kudzachokera lamulo+ ndipo ndidzachititsa chigamulo changa kukhazikika monga kuwala kwa mitundu ya anthu.+
5 Chilungamo changa chili pafupi.+ Chipulumutso+ chochokera kwa ine chili m’njira ndipo manja anga adzaweruza mitundu ya anthu.+ Zilumba zidzayembekezera ine+ ndipo zidzadikira dzanja langa.+