13 “Pali chinthu china chimene anthu inu mukuchita ndipo chikuchititsa kuti guwa lansembe la Yehova lidzaze ndi misozi, kulira ndi kubuula. Chifukwa cha zimenezi, nsembe zanu zimene mumapereka ngati mphatso n’zosavomerezeka kwa iye ndipo sakusangalala ndi chilichonse chochokera m’manja mwanu.+