14 Choncho Mawu ameneyo anakhala ndi thupi+ la nyama ndi kukhala pakati pathu, ndipo tinaona ulemerero wake, ulemerero wa mwana wobadwa yekha+ kwa bambo ake. Anali wodzaza ndi kukoma mtima kwakukulu ndi choonadi.+
16 Ndithudi, pamene ifeyo tinakudziwitsani za mphamvu ya Ambuye wathu Yesu Khristu ndi za kukhalapo* kwake,+ sitinatengere nkhani zabodza zopekedwa mochenjera ndi anthu,+ koma tinachita zimenezo chifukwa tinachita kuona ndi maso athu ulemerero wake.+