Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 53:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chifukwa cha kuvutika kwake, iye adzaona zabwino+ ndipo adzakhutira.+ Chifukwa cha zimene akudziwa, mtumiki wanga wolungamayo+ adzachititsa kuti anthu ambiri azionedwa olungama,+ ndipo adzasenza zolakwa zawo.+

  • Yeremiya 31:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 “Munthu sadzaphunzitsanso mnzake kapena m’bale wake+ kuti, ‘Mum’dziwe Yehova!’+ pakuti aliyense wa iwo adzandidziwa, kuyambira wamng’ono mpaka wamkulu,”+ watero Yehova. “Ine ndidzawakhululukira zolakwa zawo ndipo machimo awo sindidzawakumbukiranso.”+

  • Ezekieli 34:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Ndidzazipatsa m’busa mmodzi,+ amene ndi mtumiki wanga Davide,+ ndipo adzazidyetsa. Iye adzakhala m’busa wawo ndipo adzazidyetsadi.+

  • Danieli 9:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 “Pali milungu 70 imene yaikidwa yokhudza anthu a mtundu wako+ ndi mzinda wanu woyera,+ ndi cholinga choti athetse kuphwanya malamulo,+ athetse machimo,+ aphimbe cholakwa,+ abweretse chilungamo kuti chikhalepo mpaka kalekale,+ adinde chidindo+ pa masomphenya ndi maulosi, ndiponso kuti adzoze Malo Opatulikitsa.+

  • Luka 24:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Pamenepo anayamba kuwatanthauzira zinthu zokhudza iyeyo m’Malemba onse, kuyambira ndi Zolemba za Mose+ ndi za aneneri zonse.+

  • Chivumbulutso 19:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Pamenepo ndinagwada pansi n’kuwerama patsogolo pa mapazi ake kuti ndimulambire.+ Koma iye anandiuza kuti:+ “Samala! Usatero ayi! Inetu ndangokhala kapolo mnzako, ndi wa abale ako amene ali ndi ntchito yochitira umboni za Yesu.+ Lambira Mulungu,+ pakuti kuchitira umboni za Yesu ndiko cholinga cha maulosi.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena