12 Zinatero popeza munakwiriridwa naye limodzi mwa kubatizidwa ubatizo wofanana ndi wake,+ ndipo chifukwa choti muli naye pa ubwenzi, munaukitsidwa+ naye limodzi kudzera m’chikhulupiriro chimene muli nacho+ mu zinthu zimene zinachitika chifukwa cha mphamvu+ ya Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa.+