16 Ndithudi, pamene ifeyo tinakudziwitsani za mphamvu ya Ambuye wathu Yesu Khristu ndi za kukhalapo* kwake,+ sitinatengere nkhani zabodza zopekedwa mochenjera ndi anthu,+ koma tinachita zimenezo chifukwa tinachita kuona ndi maso athu ulemerero wake.+