7 Pamenepo Mose anauza Aroni kuti: “Pita kuguwa lansembe ndi kupereka nsembe yako yamachimo+ ndi nsembe yako yopsereza, kuti uphimbe machimo+ ako ndi a nyumba yako. Kenako uperekere nsembe anthuwa+ ndi kuwaphimbira machimo awo,+ monga mmene Yehova walamulira.”