17 Koma Aisiraeli sankamvera oweruzawo. Iwo ankachita chiwerewere ndi milungu ina ndi kuigwadira. Anasiya mwamsanga njira imene makolo awo anayendamo. Makolo awo ankamvera malamulo a Yehova,+ koma iwo sanachite zimenezo.
26 Kodi si akazi amenewa amene anachimwitsa Solomo mfumu ya Isiraeli? Pa mitundu yonse ya anthu panalibe mfumu yofanana ndi iye.+ Iye ankakondedwa ndi Mulungu wake,+ moti anamuika kukhala mfumu ya Aisiraeli onse. Koma akazi a mitundu ina anamuchimwitsa.+