Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 8:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Anatsatira dongosolo la tsiku ndi tsiku loperekera nsembe mogwirizana ndi lamulo la Mose. Nsembezo zinali za pa Masabata,+ za pa masiku amene mwezi watsopano waoneka+ ndi za pa zikondwerero zomwe zinkachitika katatu pa chaka.+ Zikondwererozo zinali Chikondwerero cha Mikate Yopanda Zofufumitsa,+ Chikondwerero cha Masabata+ ndi Chikondwerero cha Misasa.+

  • Nehemiya 10:32, 33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Kuwonjezera pamenepo, tinalonjeza kuti chaka chilichonse aliyense azipereka ndalama zasiliva zolemera magalamu 4* kuti akazigwiritse ntchito pa utumiki wapanyumba* ya Mulungu wathu.+ 33 Akazigwiritsenso ntchito pokonza mkate wosanjikiza,*+ nsembe yambewu+ yoperekedwa nthawi zonse, nsembe yopsereza yoperekedwa nthawi zonse pa Masabata+ ndi pa masiku amene mwezi watsopano waoneka,+ madyerero a pa nthawi yoikidwiratu,+ zinthu zopatulika, nsembe yamachimo+ yophimba machimo a Isiraeli komanso pa ntchito zonse zapanyumba ya Mulungu wathu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena