Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 28:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Koma mukapanda kumvera mawu a Yehova Mulungu wanu poonetsetsa kuti mukutsatira malamulo ake onse ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, mudzatembereredwa ndipo zinthu zoipa zotsatirazi zidzakuchitikirani:+

  • Yoswa 7:24, 25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako Yoswa ndi Aisiraeli onse anatenga Akani+ mwana wa Zera, limodzi ndi siliva uja, chovala chamtengo wapatali chija, mtanda wa golide uja,+ komanso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu, nkhosa, ndiponso hema wake, ndi chilichonse chomwe chinali chake, nʼkupita nawo kuchigwa cha Akori.+ 25 Ndiyeno Yoswa anati: “Nʼchifukwa chiyani watibweretsera tsoka?*+ Lero Yehova akubweretsera iweyo tsoka.” Atatero, Aisiraeli onse anayamba kuwaponya miyala+ anthuwo ndipo kenako anawatentha ndi moto.+ Umu ndi mmene anawaphera, anawaponya miyala.

  • Esitere 9:24, 25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Izi zinali choncho chifukwa Hamani+ mwana wa Hamedata, mbadwa ya Agagi,+ amene ankadana ndi Ayuda onse, anawakonzera Ayudawo chiwembu kuti awaphe.+ Ndiponso iye anachita Puri+ kapena kuti maere, nʼcholinga choti awasokoneze maganizo nʼkuwapha. 25 Koma Esitere atakaonekera kwa mfumu, mfumuyo inalemba+ lamulo lakuti: “Chiwembu chimene anakonzera Ayuda+ chimubwerere iyeyo.” Choncho Hamani komanso ana ake anawapachika pamtengo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena