Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 80:14-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Inu Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, chonde bwererani.

      Yangʼanani pansi pano muli kumwambako kuti muone,

      Ndipo samalirani mtengo wa mpesa uwu,+

      15 Mtengo umene dzanja lanu lamanja ladzala.+

      Ndipo muone mwana wanu amene munamupatsa* mphamvu kuti inu mulemekezeke.+

      16 Wawotchedwa ndi moto+ nʼkudulidwa.

      Anthu amawonongeka ndi kudzudzula kwanu.*

  • Yesaya 5:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Choncho, mofanana ndi mmene lawi la moto limapserezera mapesi

      Komanso mmene udzu wouma umayakira mʼmalawi a moto,

      Mizu yawo idzawola,

      Ndipo maluwa awo adzauluzika ngati fumbi,

      Chifukwa akana malamulo* a Yehova wa magulu ankhondo akumwamba

      Ndipo anyoza mawu a Woyera wa Isiraeli.+

  • Yeremiya 7:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Taonani! Mkwiyo wanga ndi ukali wanga zidzatsanulidwa pamalo awa,+ pamunthu, pachiweto, pamitengo yakuthengo ndi pachipatso chilichonse chochokera mʼnthaka. Mkwiyowo udzayaka ndipo sudzazimitsidwa.’+

  • Ezekieli 20:47
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 47 Uuze nkhalango yakumʼmwerayo kuti, ‘Imva mawu a Yehova. Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndikukuyatsa ndi moto.+ Motowo udzawotcha mtengo uliwonse wauwisi ndi mtengo uliwonse wouma umene uli mwa iwe. Malawi a motowo sadzazimitsidwa+ ndipo nkhope iliyonse, kuchokera kumʼmwera mpaka kumpoto idzapsa ndi moto.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena