Miyambo 15:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Kuyankha modekha* kumabweza mkwiyo,+Koma mawu opweteka amayambitsa mkwiyo.+ Agalatiya 6:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Abale, ngati munthu wapatuka nʼkuyamba kulowera njira yolakwika mosazindikira, inu amene ndi oyenerera mwauzimu, yesani kuthandiza munthu woteroyo ndi mzimu wofatsa.+ Koma pamene mukuchita zimenezi musamale,+ kuopera kuti inunso mungayesedwe.+ Aefeso 4:1, 2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Choncho ine, amene ndili mʼndende+ chifukwa cha Ambuye, ndikukuchondererani kuti muzichita zinthu mogwirizana+ ndi kuitana kumene anakuitanani. 2 Nthawi zonse muzichita zinthu modzichepetsa,*+ mofatsa, moleza mtima+ ndiponso muzilolerana chifukwa cha chikondi.+ 1 Timoteyo 6:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Koma munthu wa Mulungu iwe, thawa zinthu zimenezi. Mʼmalomwake yesetsa kukhala wachilungamo, wodzipereka kwa Mulungu, wachikhulupiriro, wachikondi, wopirira ndiponso wofatsa.+ 2 Timoteyo 2:24, 25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 24 Kapolo wa Ambuye sayenera kukangana ndi anthu. Koma ayenera kukhala wodekha kwa onse,+ woyenerera kuphunzitsa, wougwira mtima ena akamulakwira+ 25 ndiponso wotha kulangiza mofatsa anthu otsutsa+ kuti mwina Mulungu angawalole kulapa* nʼkudziwa choonadi molondola.+ 1 Petulo 3:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Koma muvomereze mumtima mwanu kuti Khristu ndi Ambuye ndiponso kuti ndi woyera. Nthawi zonse muzikhala okonzeka kuyankha aliyense amene wakufunsani za chiyembekezo chanu, koma muziwayankha mofatsa+ ndiponso mwaulemu kwambiri.+
6 Abale, ngati munthu wapatuka nʼkuyamba kulowera njira yolakwika mosazindikira, inu amene ndi oyenerera mwauzimu, yesani kuthandiza munthu woteroyo ndi mzimu wofatsa.+ Koma pamene mukuchita zimenezi musamale,+ kuopera kuti inunso mungayesedwe.+
4 Choncho ine, amene ndili mʼndende+ chifukwa cha Ambuye, ndikukuchondererani kuti muzichita zinthu mogwirizana+ ndi kuitana kumene anakuitanani. 2 Nthawi zonse muzichita zinthu modzichepetsa,*+ mofatsa, moleza mtima+ ndiponso muzilolerana chifukwa cha chikondi.+
11 Koma munthu wa Mulungu iwe, thawa zinthu zimenezi. Mʼmalomwake yesetsa kukhala wachilungamo, wodzipereka kwa Mulungu, wachikhulupiriro, wachikondi, wopirira ndiponso wofatsa.+
24 Kapolo wa Ambuye sayenera kukangana ndi anthu. Koma ayenera kukhala wodekha kwa onse,+ woyenerera kuphunzitsa, wougwira mtima ena akamulakwira+ 25 ndiponso wotha kulangiza mofatsa anthu otsutsa+ kuti mwina Mulungu angawalole kulapa* nʼkudziwa choonadi molondola.+
15 Koma muvomereze mumtima mwanu kuti Khristu ndi Ambuye ndiponso kuti ndi woyera. Nthawi zonse muzikhala okonzeka kuyankha aliyense amene wakufunsani za chiyembekezo chanu, koma muziwayankha mofatsa+ ndiponso mwaulemu kwambiri.+