Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 6
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI KU YERUSALEMU (3:6–8:4)

Nyimbo ya Solomo 6:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:7; 2:16

Nyimbo ya Solomo 6:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 7:10
  • +Nym 2:16

Nyimbo ya Solomo 6:4

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “Mzinda Wosangalatsa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:9
  • +1Mf 14:17; 15:33
  • +Sl 48:2
  • +Nym 6:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, ptsa. 19-20

    11/15/1987, tsa. 25

Nyimbo ya Solomo 6:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:15; 4:9; 7:4
  • +Nym 4:1-3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 19

Nyimbo ya Solomo 6:7

Mawu a M'munsi

  • *

    “Khangaza” ndi mtundu wa chipatso. Ena amati chimanga chachizungu.

Nyimbo ya Solomo 6:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 11:1

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    12/15/2011, tsa. 11

Nyimbo ya Solomo 6:9

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndi mwana woyera kwa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:14

Nyimbo ya Solomo 6:10

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “akuyangʼana pansi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 6:4

Nyimbo ya Solomo 6:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “mʼkhwawa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mla 2:5

Nyimbo ya Solomo 6:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “odzipereka.”

Nyimbo ya Solomo 6:13

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “gule wa Mahanaimu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 20

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 6:2Nym 1:7; 2:16
Nyimbo 6:3Nym 7:10
Nyimbo 6:3Nym 2:16
Nyimbo 6:4Nym 1:9
Nyimbo 6:41Mf 14:17; 15:33
Nyimbo 6:4Sl 48:2
Nyimbo 6:4Nym 6:10
Nyimbo 6:5Nym 1:15; 4:9; 7:4
Nyimbo 6:5Nym 4:1-3
Nyimbo 6:81Mf 11:1
Nyimbo 6:9Nym 2:14
Nyimbo 6:10Nym 6:4
Nyimbo 6:11Mla 2:5
Nyimbo 6:13Nym 1:6
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 6:1-13

Nyimbo ya Solomo

6 “Kodi wachikondi wako wapita kuti,

Iwe mkazi wokongola kwambiri kuposa akazi onse?

Kodi wachikondi wako wadzera njira iti?

Tiye tikuthandize kumufunafuna.”

 2 “Wachikondi wanga wapita kumunda wake,

Kumabedi amʼmunda a mbewu zonunkhira,

Kuti akadyetse ziweto kuminda,

Ndiponso kuti akathyole maluwa.+

 3 Wachikondi wanga, ine ndi wake

Ndipo iye ndi wanga.+

Iye akudyetsera ziweto msipu umene uli pakati pa maluwa.”+

 4 “Wokondedwa wangawe,+ ndiwe wokongola ngati Tiriza,*+

Ndiwe wooneka bwino ngati Yerusalemu,+

Ndipo ndiwe wogometsa ngati magulu a asilikali amene azungulira mbendera.+

 5 Yangʼana kumbali kuti maso ako+ asandiyangʼanitsitse,

Chifukwa akundichititsa mantha.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

Zimene zikuthamanga potsika mapiri a ku Giliyadi.+

 6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa

Zimene zikuchokera kosambitsidwa,

Zonse zabereka mapasa,

Ndipo palibe imene ana ake afa.

 7 Masaya ako munsalu yako yophimba kumutuyo

Ali ngati khangaza* logamphula pakati.

 8 Ngakhale patakhala mafumukazi 60

Komanso adzakazi* 80

Ndi atsikana osawerengeka,+

 9 Koma mmodzi yekha ndi amene ali njiwa yanga,+ wopanda chilema.

Iye ndi mwana wapadera kwambiri kwa mayi ake.

Ndi mwana amene amakondedwa ndi* mayi amene anamubereka.

Ana aakazi akamuona, amamunena kuti ndi wosangalala.

Mafumukazi ndi adzakazi amamutamanda.

10 ‘Kodi mkazi amene akuwala* ngati mʼbandakuchayu ndi ndani,

Amene ndi wokongola ngati mwezi wathunthu,

Wosadetsedwa ngati kuwala kwa dzuwa,

Wogometsa ngati magulu a asilikali amene azungulira mbendera?’”+

11 “Ine ndinapita kumunda wa mitengo ya zipatso zokhala ndi mtedza,+

Kuti ndikaone ngati yaphuka masamba atsopano mʼchigwa,*

Kuti ndikaone ngati mitengo ya mpesa yaphukira,

Ndiponso ngati mitengo ya makangaza yachita maluwa.

12 Mosazindikira,

Chifukwa cholakalaka kuona zinthu zimenezi, ndinakafika

Kumene kunali magaleta a anthu olemekezeka* a mtundu wanga.”

13 “Bwerera, bwerera iwe Msulami!

Bwerera, bwerera

Kuti tione kukongola kwako!”

“Nʼchifukwa chiyani mukuyangʼanitsitsa Msulami?”+

“Iye ali ngati gule wa magulu awiri a anthu.”*

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena