Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g99 10/8 tsamba 31
  • Chinthu Chamtengo Wapatali Kuposa Ndalama

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chinthu Chamtengo Wapatali Kuposa Ndalama
  • Galamukani!—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Anthu Oona Mtima Amatamanditsa Yehova
    Nsanja ya Olonda—2005
  • Latvia Alabadira Uthenga Wabwino
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Kodi Ndiyenera Kudziwa Zotani Zokhudza Nkhanza za Kugonana?​—Gawo 2: Zimene Mungachite Ngati Munachitidwapo Nkhanza Zotere
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Sanali Wokalamba Kwambiri Kosakhoza Kutumikira Yehova
    Nsanja ya Olonda—1994
Onani Zambiri
Galamukani!—1999
g99 10/8 tsamba 31

Chinthu Chamtengo Wapatali Kuposa Ndalama

YOSIMBIDWA NDI MTOLANKHANI WA GALAMUKANI! KU CANADA

“[Iye] anapatsa mwana wake wamkazi mphatso yamtengo wapatali kuposa kuchuluka kwa ndalama zonse,” inatero ndemanga ya mkonzi wa nyuzipepala yotchedwa The Monitor ya ku Bridgetown, Nova Scotia. Kodi mphatsoyo inali chiyani? Inali “chitsanzo chapadera cha kuona mtima” kwake.

Anna ndi mwana wake wamkazi Tanya anaima panyumba ya munthu pamene panali selo ndipo anagula kachikwama kakang’ono koyera kuti Tanya aziikamo Baibulo lake. Atafika kunyumba, Tanya anatsegula zipi yam’kati mwa kachikwamako ndipo anadadwa kupeza kuti munali ndalama zokwana $1,000 zamapepala. Nthaŵi yomweyo mayi ake ndi iye anabwerera kupita kunyumba kuja kukapereka ndalama zonse kwa mzimayi yemwe anagulako kachikwamako. Zikuoneka kuti, kachikwamako sanali kukagwiritsa ntchito kaŵirikaŵiri ndipo kanali ka malemu amayi ake a mzimayiyo, omwe anamwalira ndi matenda a ku ubongo, ndipo sanayang’anemo kaye asanakagulitse. M’mawu ake othokoza zedi, mzimayiyo anati: “Zimenezi zandiyambitsanso kukhulupirira anthu . . . N’zolimbikitsa kudziŵa kuti anthu oona mtima adakalipobe.”

Patsamba loyamba la nyuzipepala yakumaloko panali nkhani yomweyi ndipo nyuzipepalayi inagwira mawu a Anna akumati: “Ife monga Mboni za Yehova, limenelo ndilo khalidwe lathu. Tili ndi [chikumbumtima] chozikidwa m’Baibulo. Tikufunanso kuphunzitsa Tanya khalidwe labwino.” Kwa Tanya, kachikwama kake koyera katsopanoko kadzakhala chikumbutso chapadera cha phunziro la kuona mtima.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena