Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 8/07 tsamba 28
  • Ubwino Wophunzitsa Ana Mawu a Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ubwino Wophunzitsa Ana Mawu a Mulungu
  • Galamukani!—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Sukulu Yopambana Yapadziko Lonse
    Galamukani!—1996
  • Sukulu ya Utumiki Wateokalase Imapindulitsa
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kuphunzitsa Atumiki a Ufumu
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulira
  • Sukulu Imene Imatikonzekeretsa Kuchita Zinthu Zimene Zili Zofunika Kwambiri
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Galamukani!—2007
g 8/07 tsamba 28

Ubwino Wophunzitsa Ana Mawu a Mulungu

Makolo amene amachita khama kuphunzitsa ana awo kuyambira ali aang’ono amapindula. Mwachitsanzo, Dorian, mwana wamng’ono wa ku Peru, ku South America, anakamba nkhani yake yoyamba mu Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ku Nyumba ya Ufumu ya Mboni za Yehova ali ndi zaka zinayi. Atayamba kupita ku sukulu, ankatha kufotokozera aphunzitsi ndi anzake chifukwa chake sakondwerera Khirisimasi powawerengera Baibulo.

Posachedwapa, ali ndi zaka zisanu, Dorian anapemphedwa kulankhula ndi ana a sukulu onse pafupifupi 500 kuti afotokoze maganizo ake pankhani ya Tsiku la Abambo. Anakonza nkhani yamphindi 10 yamutu wakuti “Udindo wa Abambo,” kuchokera m’Baibulo pa Aefeso 6:4. Pomaliza nkhani yakeyo, anati: “M’malo mokumbukira Tsiku la Abambo kamodzi pachaka, ana ayenera kumvera ndi kulemekeza makolo awo tsiku lililonse.”

Sukulu ya Utumiki wa Mulungu inayamba m’chaka cha 1943 ndi cholinga chophunzitsa ana ndi akulu omwe kulankhula bwino pagulu, ndipo yakhala ikuchitika kamodzi pamlungu kumisonkhano ya Mboni za Yehova. Kuchokera nthawi imeneyo, sukuluyi yapereka maphunziro a m’Baibulo kuwonjezera pa malangizo amene makolo amapemphedwa kupereka kwa ana awo.—Miyambo 22:6.

Simon wa ku Switzerland, anayamba kuwerenga Baibulo mu Sukulu ya Utumiki wa Mulungu mu November 2005, ali ndi zaka 6. Chaka chotsatira, anafunsidwa mafunso pamsonkhano waukulu wa Mboni za Yehova. Kodi amaona bwanji zinthu zauzimu?

Simon amakonda misonkhano yachikhristu. Zili choncho chifukwa chakuti amayesetsa kusaphonya msonkhano uliwonse, ngakhale ngati atatopa. Ndiponso, amapita kukalalikira ndi abale ake. Mwezi uliwonse, amagawira magazini mwina 30 kapena mpaka 50 a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! kwa anthu amisinkhu yonse. Komanso, amauza bambo ake za m’Baibulo ndi kuwalimbikitsa kupita nawo kumisonkhano.

Zoonadi, makolo amene amalera ana awo “m’malango a Yehova ndi kuwaphunzitsa kalingaliridwe kake” amasangalala kwambiri anawo akamalabadira ndi kubala chipatso chachilungamo.—Aefeso 6:4; Yakobe 3:17, 18.

[Chithunzi patsamba 28]

Dorian ali ku sukulu

[Chithunzi patsamba 28]

Simon ali ku Nyumba ya Ufumu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena