Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 2 tsamba 10-11
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Abwino Amavutika?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’chifukwa Chiyani Anthu Abwino Amavutika?
  • Galamukani!—2020
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Chifukwa Chake Kudziwa Yankho la Funsoli Kuli Kofunika
  • Taganizirani Izi
  • Zimene Baibulo Limanena
  • Kodi Tinalengedwa Kuti Tizivutika?
    Galamukani!—2020
  • Mavuto
    Galamukani!—2015
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Nkhani Zimene Zili M’magaziniyi
    Galamukani!—2020
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 2 tsamba 10-11
Makolo akuyang’ana mwana wawo yemwe wagona pabedi kuchipatala, atamudula mbali ina ya dzanja lake.

3. N’chifukwa Chiyani Anthu Abwino Amavutika?

Chifukwa Chake Kudziwa Yankho la Funsoli Kuli Kofunika

Zimaoneka kuti n’zopanda chilungamo kuti anthu abwino azivutika. Zimenezi zimachititsa anthu ena kuona kuti palibe chifukwa chokhalira munthu wabwino.

Taganizirani Izi

Anthu ena amakhulupirira kuti munthu akafa amakabadwanso. Iwo amanena kuti munthu amene ankachita zabwino akabadwanso amakhala ndi moyo wabwino, koma amene ankachita zoipa akabadwanso amakhala moyo wovutika. Malinga ndi zimene anthuwa amakhulupirira, ngakhale munthu atakhala wabwino pano, akhoza kumakumanabe ndi mavuto ngati ankachita zinthu zoipa “m’moyo wa m’mbuyomu.” Komabe . . .

  • Kodi cholinga cha kuvutikaku chingakhale chiyani popeza munthu amene akuti akafa amabadwanso, sakumbukira n’komwe zimene ankachita m’moyo wa m’mbuyomu?

  • N’chifukwa chiyani panopa timayesetsa kukhala ndi moyo wathanzi komanso kupewa ngozi, chonsecho tikhoza kumavutikabe chifukwa cha zinthu zoipa zimene tinkachita m’moyo wa m’mbuyomu?

    KUTI MUDZIWE ZAMBIRI

    Onerani vidiyo yakuti N’chifukwa Chiyani Mulungu Amalola Kuti Anthu Azivutika? pa jw.org.

Zimene Baibulo Limanena

Kuvutika si chilango chochokera kwa Mulungu.

Koma m’malomwake zimangochitika, ndipo nthawi zambiri zimachitika chifukwa choti tili pamalo olakwika komanso pa nthawi yolakwika.

“Anthu othamanga kwambiri sapambana pampikisano, amphamvu sapambana pankhondo, anzeru sapeza chakudya, omvetsa zinthu nawonso sapeza chuma, ndipo ngakhale odziwa zinthu sakondedwa, chifukwa nthawi yatsoka ndi zinthu zosayembekezereka zimagwera onsewo.”​—MLALIKI 9:11.

Uchimo umachititsanso kuti tizivutika.

Nthawi zambiri anthu akamanena kuti “tchimo” amatanthauza zinthu zoipa zimene munthu amachita. Komabe Baibulo limagwiritsa ntchito mawuwa potanthauza za uchimo umene anthu onse, abwino ndi oipa omwe, anatengera.

“Anandilandira mu zowawa za pobereka ndili wochimwa. Ndipo ndine wochimwa kuchokera pamene mayi anga anatenga pakati panga.”​—SALIMO 51:5.

Uchimo wabweretsa mavuto ambiri kwa anthu.

Wachititsa kuti anthufe tisakhale pa ubwenzi wabwino ndi Mlengi wathu komanso wachititsa kuti tisamagwirizane ndi anzathu, tizikhala ndi maganizo oipa, komanso kuti tiwononge dzikoli. Zimenezi zachititsa kuti anthu onse azikumana ndi mavuto ambiri.

“Pamene ndikufuna kuchita chinthu chabwino, choipa chimakhala chili ndi ine.”​—AROMA 7:21.

“Chilengedwe chonse chikubuula limodzi ndi kumva zowawa.”​—AROMA 8:22.

N’chifukwa chiyani anthu abwino amavutika?

Mavuto ambiri omwe timakumana nawo amachitika chifukwa cha uchimo umene anthu tonse, abwino ndi oipa omwe, tinatengera. Chifukwa cha uchimowu, timadwala matenda osiyanasiyana kuphatikizapo matenda ovutika maganizo komanso umachititsa anthu ena kukhala ndi makhalidwe oipa, omwe amavulaza nawo anzawo.

Kodi cholinga cha Mulungu potilenga chinali choti tizivutika?

Onani funso 4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena