Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g25 No. 1 tsamba 4-5
  • Zinthu Zina Zimafunika Kungovomereza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zinthu Zina Zimafunika Kungovomereza
  • Galamukani!—2025
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?
  • ZIMENE MUNGACHITE
  • Kukwera Mitengo Kwa Zinthu Padziko Lonse—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
  • Zimene Zili M’magaziniyi
    Galamukani!—2025
  • Kukwera kwa Mitengo—Mtengo wa Munthu
    Galamukani!—1989
  • Muziyembekezera Kuti Zinthu Zidzasintha
    Galamukani!—2025
Onani Zambiri
Galamukani!—2025
g25 No. 1 tsamba 4-5
Zithunzi: 1. Mzimayi akusankha tomato pamsika. 2. Akulipira zinthu zimene wagula.

ZIMENE MUNGACHITE PA VUTO LA KUKWERA MITENGO KWA ZINTHU

Zinthu Zina Zimafunika Kungovomereza

Mitengo ya zinthu ikamakwera pang’onopang’ono mwina sitingazindikire, makamaka ngati malipiro athunso akukwera. Koma ngati mitengo yakwera kamodzin’kamodzi ndipo malipiro athu sanasinthe, tingayambe kuda nkhawa, makamaka ngati tili ndi banja.

Sitingaletse kuti zinthu zisakwere. Koma kungovomereza kuti zinthu zakwera mitengo, kungatithandize.

N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?

Anthu amene amadziwa kuti sangaletse kukwera mitengo kwa zinthu, savutika . . .

  • kukhalabe odekha. Tikakhala odekha, timaganiza bwino komanso timasankha zinthu mwanzeru.

  • kupewa kuchita zinthu zosathandiza. Mwachitsanzo, zingakhale zosathandiza kuzemba kulipira mabilu kapena kuwononga ndalama pa zinthu zosafunika.

  • kupewa kukangana ndi anthu am’banja lathu pa nkhani za ndalama.

  • kupeza njira zothandiza kupirira vutoli zomwe zingaphatikizepo kugwiritsa ntchito ndalama zochepa komanso kuona zinthu zimene tikufunikadi kugula.

ZIMENE MUNGACHITE

Muzikhala okonzeka kusintha. Zinthu zikakwera mitengo, ndi nzeru kuchepetsa zimene timagula, ngati zingatheke. Anthu ena amafuna kuti azikhalabe moyo wapamwamba kuposa ndalama zimene amapeza. Choncho amakhala ngati akuyesa kusambira mumtsinje umene madzi ake akuthamanga kwambiri. Kuchita zimenezi kumangowatopetsa. Ngati muli ndi banja, muyenera kuti mumadera nkhawa za mmene mungapezere zofunika pa moyo za banja lanu ndipo izi n’zomveka. Koma kumbukirani kuti anthu am’banja lanu amafuna chikondi chanu komanso nthawi yanu kuposa china chilichonse.

“Ndi ndani wa inu amene angatalikitse moyo wake pangʼono pokha chifukwa cha kuda nkhawa?”—Luka 12:25.

“Musamadere nkhawa za mawa, chifukwa mawalo lidzakhala ndi zodetsa nkhawa zakenso. Mavuto a tsiku lililonse ndi okwanira pa tsikulo.”—Mateyu 6:34.

Kufuna kumakhalabe moyo wapamwamba zinthu zitakwera mtengo, kuli ngati kuyesa kusambira mumtsinje umene madzi ake akuthamanga kwambiri

Phazilya.

“Baibulo linaneneratu pa 2 Timoteyo 3:1, kuti tikukhala ‘m’nthawi yapadera komanso yovuta.’ Choncho sindimadabwa ndi mavuto azachuma komanso kukwera mitengo kwa zinthu. Ndimangoyesetsa kusintha n’kupeza njira yomwe ingandithandize kuti ndisamagule zinthu zosafunika kwenikweni.”—Phazilya, Azerbaijan.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena