Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g25 No. 1 tsamba 6-9
  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama Zanu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama Zanu
  • Galamukani!—2025
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?
  • ZIMENE MUNGACHITE
  • Zimene Mungachite Ngati Mukupeza Ndalama Zochepa
    Nkhani Zina
  • 2 | Muzisamala Ndalama
    Galamukani!—2022
  • Mmene Mungapeŵere Kukhala m’Ngongole
    Galamukani!—1997
  • Kodi Ndingatani Kuti Ndizisamala Ndalama?
    Galamukani!—2006
Onani Zambiri
Galamukani!—2025
g25 No. 1 tsamba 6-9
Zithunzi: 1. Makolo akupanga bajeti ndipo mwana wawo ali chapafupi kukhitchini. 2. Foni ili pamwamba pamalisiti ndi mabilu ndipo zikuoneka kuti amawerengetserapo ndalama.

ZIMENE MUNGACHITE PA VUTO LA KUKWERA MITENGO KWA ZINTHU

Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama Zanu

Tonsefe timavutika ndi kukwera mitengo kwa zinthu. Koma sikuti tilibiretu mtengo wogwira. Pali zinthu zina zimene mungachite kuti zinthu ziziyendako bwino.

N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?

Ngati simungagwiritse ntchito ndalama zanu mwanzeru, ndalamazo zikhoza kutha mosadziwika bwino ndipo izi zingakuwonjezereni nkhawa. Ngakhale zitakhala kuti mumapeza ndalama zochepa, pali zinthu zina zimene mungachite zomwe zingakuthandizeni.

ZIMENE MUNGACHITE

Muzikhala moyo wogwirizana ndi ndalama zimene mumapeza. Mukamachita zimenezi, mtima wanu uzikhala m’malo ndipo simungavutike ngati patagwa zadzidzidzi.

Kuti musamagwiritse ntchito ndalama zambiri kuposa zimene mumapeza, muyenera kukhala ndi bajeti. Mukamakonza bajetiyo, muziganizira zinthu zofunika kwambiri. Ndiye muziyesetsa kutsatira bajeti yanuyo, ndipo muzisintha ngati mitengo ya zinthu yakwera kapena ngati ndalama zimene mumapeza zasintha. Ngati muli pa banja, muzikambirana ndi mwamuna kapena mkazi wanu mukamapanga bajeti.

Tayesani izi: Ngati n’zotheka, muzipewa kugula zinthu pa ngongole. Anthu ambiri amaona kuti kuchita zimenezi kumawathandiza kuti azigula zinthu zomwe zili pabajeti komanso azipewa ngongole. Komanso muzipeza nthawi yoona masitetimenti anu akubanki. Kudziwa ndalama zimene mwatsala nazo kungakuthandizeni kuti muchepetse nkhawa.

Kukhala moyo wogwirizana ndi ndalama zimene mumapeza kungakhale kovuta. Koma kukhala ndi bajeti yabwino kungakuthandizeni kwambiri. Kungakuthandizeninso kuti musamangokhalira kudera nkhawa nkhani zokhudza ndalama.

‘Muziwerengera ndalama zimene mungawononge.’—Luka 14:28.


Muzichita zinthu mosamala kuti musachotsedwe ntchito. Kodi mungatani kuti musachotsedwe ntchito? Zina zomwe mungachite ndi izi: Muzifika kuntchito pa nthawi yake ndipo muzikhala ndi maganizo oyenera okhudza ntchito yanu. Muzithandiza ena, muzilimbikira ntchito, muzichita zinthu mwaulemu, muzitsatira malamulo a ntchito yanu komanso muziwonjezera luso lanu.


Muzipewa kuwononga ndalama. Dzifunseni kuti, ‘Kodi ndimawononga ndalama pa zinthu zosathandiza?’ Mwachitsanzo, anthu ena amawononga ndalama zomwe azivutikira, pa zinthu monga kugwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo, juga, kusuta kapena kumwa mowa mwauchidakwa. Makhalidwe amenewa akhozanso kuwononga thanzi la munthu komanso kuchititsa kuti achotsedwe ntchito.

“Wosangalala ndi munthu amene amapeza nzeru. . . . Chifukwa kupeza nzeru nʼkwabwino kuposa kupeza siliva.”—Miyambo 3:​13, 14.


Muzisunga ndalama kuti mudzagwiritse ntchito pa zinthu zadzidzidzi. Ngati mungathe, muzisunga ndalama zoti mudzagwiritse ntchito pa zinthu zadzidzidzi. Ndalama zimenezo zingathandize kuti musade nkhawa kwambiri ngati inuyo kapena munthu wina wa m’banja lanu atadwala, mutachotsedwa ntchito kapena patachitika vuto lina losayembekezereka.

“Nthawi yatsoka komanso zinthu zosayembekezereka zimagwera [tonsefe].”—Mlaliki 9:11.

Zimene zingakuthandizeni kuti muzisunga ndalama

M’botolo lagalasi muli ndalama.

Muzikonda kuphika nokha chakudya m’malo mokagula.

Ngati mumakonda kukadya kulesitanti kapena kugula zakumwa ndi zakudya zophikaphika, mukhoza kumawononga ndalama zambiri. N’zoona kuti pamafunika nthawi komanso mphamvu kuti muphike nokha chakudya, koma mungapulumutse ndalama zambiri. Zingathandizenso kuti muzitha kuphika chakudyacho mmene mukufunira.

Muzigula zinthu mwanzeru.

  • Muzikhala ndi mndandanda wa zimene mukufuna kugula. Musamagule zinthu zosakonzekera.

  • Ngati mungakwanitse, muzigula zinthu motchipa pogula zambiri nthawi imodzi. Komabe muzitsimikizira kaye kuti mungathe kuzisunga bwinobwino kuti zisawonongeke.

  • Mukhozanso kumagula zinthu zamakampani omwe katundu wawo amakhala wotchipirapo ngati zinthuzo ndi zabwinobwino.

  • Ngati kwanuko zimatheka kugula zinthu kudzera pa intaneti, onani ngati mungathe kuchita zimenezi. Zingathandize kuti muzipeza zinthu zotchipa, musamagule zinthu zosakonzekera komanso kuti muzidziwa mosavuta mmene mwagwiritsira ntchito ndalama zanu.

  • Mungachitenso bwino kugula zinthu pa nthawi yomwe kuli selo kapena pamene zatsika mtengo. Muziyerekezera kaye mitengo ya zinthu m’mashopu osiyanasiyana ndipo m’madera ena zimakhala zothandiza kuchitanso chimodzimodzi ndi mitengo ya magetsi komanso madzi.

Musamafulumire kugula zinthu zapamwamba ngati muli kale ndi zina.

Opanga mafoni komanso zinthu zina amapanga mamodelo atsopano n’cholinga choti awonjezere phindu lomwe amapeza. Choncho dzifunseni kuti: ‘Kodi kugula modelo yatsopano kundithandizadi ineyo? Kodi ndikufunikiradi kuchita zimenezi panopa? Ngati ndikufunika kugula china, kodi ndikufunika cha modelo yatsopano?’

Muzikonzetsa zinthu zowonongeka m’malo mogula zina.

Zinthu zoyendera magetsi zizionedwa pafupipafupi kuti zikhale nthawi yaitali. Zikawonongeka, ngati kugula zina kungafune ndalama zambiri muzingokonzetsa zomwezo. Mukhozanso kungogula zinthu kwa anthu m’malo mokagula zatsopano kushopu.

Muzilima nokha zakudya.

Yesani kumalima nokha zakudya. Kuchita zimenezi kungathandize kuti mupulumutse ndalama, muzitha kugulitsa zakudya zina komanso muzipatsako ena.

“Mapulani a munthu wakhama amamuthandiza kuti zinthu zimuyendere bwino.”—Miyambo 21:5.

Khadi la ngongole.

“Nthawi zonse timaona mitengo ya zinthu zomwe timagula komanso timasamala kwambiri ndi mmene timagwiritsira ntchito khadi lathu la ngongole.”—Miles, England.

Kakope, cholembera ndiponso makiyi a galimoto.

“Tisanapite kukagula zinthu, ine ndi anthu am’banja langa timalemba kaye zinthu zomwe tikufunikira.”—Jeremy, U.S.A.

Kakope kolembamo zofunika kugula ndiponso chowerengetsera ndalama.

“Nthawi zonse timakonzanso bajeti yathu kuti igwirizane ndi mmene mitengo ya zinthu ilili. Komanso timasunga kandalama kena kuchitira patagwa zadzidzidzi.”—Yael, Israel.

Sipanala ndi sikuludilaiva.

“Tinaphunzitsa ana athu kuti azikonza okha zinthu zomwe zawonongeka m’malo mogula zatsopano. Zimenezi zikuphatikizapo galimoto yathu komanso zipangizo zoyendera magetsi. Ine ndi mkazi wanga timapewanso kugula zinthu zomwe zangotuluka kumene.”—Jeffrey, U.S.A.

“Ndimapulumutsa ndalama polima ndekha ndiwo zamasamba komanso kuweta nkhuku. Ndimakwanitsanso kugawirako ena masamba omwe ndimalima.”—Hono, Myanmar.

Mzimayi akuthyola ndiwo zamasamba pakadimba.
    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena