Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/96 tsamba 2
  • Konzekerani Ntchito ya Kugaŵira Sabusikripishoni mu April

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Konzekerani Ntchito ya Kugaŵira Sabusikripishoni mu April
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Tingapange Mwezi wa April 2000 Kukhala Mwezi Wathu Wabwino Kuposa Yonse?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • April—Nthaŵi ‘Yogwiritsitsa Ntchito ndi Kuyesetsa’
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Kodi Mungawonjezere Chitamando Chanu kwa Yehova m’April?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
km 2/96 tsamba 2

Konzekerani Ntchito ya Kugaŵira Sabusikripishoni mu April

Monga momwe taonera mu Kalenda yathu ya 1996, Mgonero wa Ambuye chaka chino udzachitidwa pa April 2. Pokhala olimbikitsidwa ndi chochitika chapadera chimenechi, aliyense adzakhaletu ndi phande mwachangu m’kugaŵira sabusikripishoni mu April yense. Tidzakhala tikugaŵira magazini apanthaŵi yake abwino chotani nanga! Nsanja ya Olonda ya April 1 idzasimba za nkhani yapoyera ya msonkhano wachigawo wa chaka chatha yakuti, “Tamandani Mfumu Yamuyaya!” Nsanja ya Olonda ya April 15 idzakhala ndi mutu wankhani yapoyera yapadera ya April wapita wakuti “Mapeto a Chipembedzo Chonyenga Ayandikira.” Nkhani yapadera ya chaka chino pa April 21 yakuti, “Kukhala Opanda Banga Pakati pa Mbadwo Wokhotakhota,” idzatisonkhezera mowonjezereka. Tidzagaŵira Galamukani! wa May 8 wa mutu wakuti “Pamene Sikudzakhalanso Nkhondo.”

Monga chinthu chotsatira pa mkupiti wa Uthenga wa Ufumu wa April wathayo, April yemwe akubwerayo ayenera kukhala mwezi wapadera wa kugaŵira sabusikripishoni. Inoyo ndiyo nthaŵi ya kupanga makonzedwe. Ambiri adzafuna kulembetsa kukhala apainiya othandiza. Makope apadera ofunika kaamba ka magazini a April ayenera kuodedwa. Makonzedwe a Masiku a Magazini angapangidwe, aliyense akumatengamo mbali ngati kuli kotheka—mmaŵa, masana, ndi/kapena madzulo. Tiyeni tonsefe ‘tikhale akuchita mawu.’ Monga momwe kunanenedweratu ponena za Mesiya pa Salmo 69:9, nafenso tikhozetu kunena kuti: “Changu cha pa nyumba yanu chandidya ine.”—Yak. 1:22; Yoh. 2:17.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena