Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/98 tsamba 7
  • Kodi Mukulinganiza Kudzatani m’Chilimwe?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mukulinganiza Kudzatani m’Chilimwe?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Nkhani Yofanana
  • Apainiya Othandiza 3,000 Akufunika
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • ‘Chitirani Umboni Bwino Lomwe za Uthenga Wabwino’
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Lengezani Ulemerero wa Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
km 5/98 tsamba 7

Kodi Mukulinganiza Kudzatani m’Chilimwe?

1 Kodi si zoona kuti tingafikire zolinga zathu zopindulitsa ngati tikonzekera mmene tingagwiritsirire ntchito bwino kwambiri nthaŵi yathu? Miyezi ikudzayi ingatipatse mipata yosiyanasiyana yakufikira zolinga zateokrase. (Miy. 21:5) Kodi zina mwa zimenezo nziti?

2 Msonkhano wakuti “Njira ya Moyo ya Mulungu” uli chochitika chimodzi chimene tonsefe tiyenera kuchiphatikiza polinganiza zinthu zathu chilimwe chino. Pemphani nthaŵi kuntchito kapena kusukulu kuti tsiku lililonse la msonkhanowo mudzapezekepo.

3 Bwanji osalinganiza kudzaonjezera utumiki wanu wakumunda m’miyezi ikudzayi, poti tsopano nyengo yadzinja yatha, mungakhale ndi nthaŵi yambiri yowonongera pantchito yolalikira. Maholide a sukulu adzapatsa achinyamata mpata wakuchita upainiya wothandiza m’mwezi umodzi kapena ingapo ikudzayo. Enanso angalinganiziretu kudzachita upainiya wothandiza m’August, poti padzakhala milungu isanu yathunthu ndi maholide aŵiri. Mmene tizitsiriza chaka chautumiki August uno, tidzayesetsa ndithu kuti aliyense agwire nawo ntchito kwambiri mu utumiki.

4 Kodi mukulinganiza kudzathandiza mpingo wina wapafupi womwe ukufuna chithandizo pofola gawo lake? Woyang’anira dera angauze akulu zimene zikufunikira m’dera lanu. Kapena, ngati mungayenerere, ndipo mwina mungakonde kufunsira ku Sosaite kuti mukafole gawo losafoledwafoledwa kapena lopanda munthu, pemphani fomu kwa akulu anu. Ngati mudzakhala paholide kutali ndi kwanu, linganizani kudzamapezeka pamisonkhano ndi kuloŵa nawo mu utumiki wakumunda ndi mpingo wakomweko. Ngati mudzakachezera achibale omwe sali Mboni za Yehova, linganizani pasadakhale njira zimene mungakawauzire choonadi.

5 Kodi mukulinganiza kudzatani m’miyezi ikudzayi? Mosakayikira, mungakonde kuti mupume. Komabe musanyalanyaze mipata yambiri yomwe ilipo imene ingakulimbikitseni mwauzimu mwa kufunafunabe Ufumu choyamba.—Mat. 6:33; Aef. 5:15, 16.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena