Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/07 tsamba 1
  • Yendani Monga Anthu Anzeru

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yendani Monga Anthu Anzeru
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • M’minda Mwayera Kale Ndipo M’mofunika Kukolola
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Muzigwira Nawo Mokwanira Ntchito Yokolola Mwauzimu
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Ndife Osangalala Kutumikira Yehova Modzipereka
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Kulengeza Choonadi Tsiku ndi Tsiku Motsanzira Yesu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 11/07 tsamba 1

Yendani Monga Anthu Anzeru

1 Yesu atapempha asodzi anayi kuti akhale otsatira ake, iwo sanazengereze koma ‘nthawi yomweyo anamutsatira.’ (Mat. 4:18-22) Saulo wa ku Tariso atatembenukira ku Chikhristu n’kuyambanso kupenya, iyenso sanachedwe koma “nthawi yomweyo anayamba kulalikira za Yesu m’masunagoge.” (Mac. 9:20) Nthawi sibwerera m’mbuyo, imati ikadutsa yadutsa. N’chifukwa chake n’kofunika kuti ‘tiziyenda monga anthu anzeru’ pankhani yogwiritsa ntchito nthawi yathu.—Aef. 5:15, 16.

2 Zongotigwera: Mwayi wotumikira Yehova womwe tili nawo lero mwina mawa sitingakhale nawo. (Yak. 4:14) Aliyense zinazake zikhoza ‘kum’gwera’ mwadzidzidzi. (Mlal. 9:11) Komanso, aliyense akunka nakalamba, ndipo m’dongosolo lino la zinthu, sitingapewe “masiku oipa” amene amadza ndi ukalamba ndiponso amene amatilepheretsa kuchita zambiri muutumiki wa Yehova. (Mlal. 12:1) Choncho, ndi nzeru kudzipereka kwa Mulungu mwamsanga m’malo mozengereza. Ndiponso si chinthu chanzeru kuganiza kuti tidzawonjezera utumiki zinthu zonse zikadzakhala bwino. (Luka 9:59-62) Abulahamu anapeza mtendere m’zaka za ukalamba wake, ndipo anafa ‘m’ukalamba wabwino’ chifukwa choti moyo wake anaugwiritsa ntchito mwanzeru mwakudzipereka ndi mtima wonse kwa Yehova.—Gen. 25:8.

3 Nthawi Yafupika: Timafunikanso kugwiritsa ntchito nthawi yathu mwanzeru chifukwa “nthawi yotsalayi yafupika.” (1 Akor. 7:29-31) Posachedwapa dongosolo la zinthu lilipoli litha. Nawonso mwayi wosonkhanitsa nawo anthu onga nkhosa m’nthawi ‘yokolola za dziko lapansi’ utha. (Chiv. 14:15) Motero, tiyenera kusamala kuti nkhawa za moyo ndiponso zinthu zina zotanganitsa zisatitayitse nthawi imene tikanathera mu utumiki. (Luka 21:34, 35) Zidzakhalatu zosangalatsa kwambiri kuganizira kuti tinagwira nawo mokwanira ntchito yokolola imeneyi.

4 Tiyenera kukhala tcheru nthawi zonse kuti tisaphonye mwayi wabwino wa utumiki umene tingaupeze. Tiyeni tikhale otsimikiza kuchita zonse zomwe tingathe kuti titumikire Yehova ‘nthawi iliyonse imene tikuti “Lero.”’ (Aheb. 3:13) Tikatero, tidzasonyeza kuti ndifedi anzeru, chifukwa “wochita chifuniro cha Mulungu akhalabe kosatha.”—1 Yoh. 2:17.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena